1Yehova akuti, “ ‘Pa nthawi imeneyo, mafupa a mafumu ndi a akuluakulu a ku Yuda, mafupa a ansembe ndi a aneneri, ndiponso mafupa a anthu a ku Yerusalemu adzafukulidwa.
2Adzawamwaza pa nthaka kuyangʼana dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zonse zamlengalenga, zimene ankazikonda, kuzitumikira ndi kuzitsatira, kupemphako nzeru ndiponso kuzilambira. Mafupawo sadzawasonkhanitsa kapena kuwakwirira, koma adzakhala ngati ndowe pamwamba pa nthaka.
3Otsala onse a mtundu woyipawu adzafuna imfa kopambana moyo kulikonse kumene ndidzawapirikitsirako, akutero Yehova Wamphamvuzonse.’ ”
4“Tsono awuze anthuwa, ‘Yehova akuti:
5Chifukwa chiyani nanga anthu awa akupitirirabe kuchimwa, osabwerera?
6Ine ndinatchera khutu kumvetsera
7Mbalame yotchedwa kakowa ija imadziwa
8“ ‘Inu mukunena bwanji kuti,
9Anthu anzeru achita manyazi;
10Nʼchifukwa chake akazi awo ndidzawapereka kwa amuna ena
11Iwo amapoletsa zilonda za anthu anga
12Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazi?
13“ ‘Ndidzatenga zokolola zawo,
14Koma amati, “Tikukhala pano chifukwa chiyani?
15Tinkayembekezera mtendere
16Kulira kwa ngʼombe zazimuna za mdani
17Yehova akuti, “Onani, ndikukutumizirani njoka zaululu,
18Ndadzazidwa ndi chisoni kwambiri,
19Imvani kulira kwa anthu anga
20“Nthawi yokolola yapita,
21Chifukwa cha mavuto a anthu anga, ine ndikumva kuwawa;
22Kodi ku Giliyadi kulibe mankhwala ochiritsa?