We Believe JesusFé, Esperança e Nova Vida

Yeremiya 17

Biblica® Tsekulani Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero · nianja

← Yeremiya 16 Yeremiya Yeremiya 18 →

1“Tchimo la Yuda lazokotedwa ndi cholembera cha chitsulo,

2Ngakhale ana awo amakumbukira

3Chuma chanu ndiponso katundu wanu yense

4Mudzataya dziko limene ndinakupatsani

5Yehova akuti,

6Munthuyo adzakhala ngati chitsamba mʼchipululu;

7“Koma ndi wodala munthu amene amadalira Yehova,

8Adzakhala ngati mtengo wodzalidwa mʼmphepete mwa madzi

9Mtima wa munthu ndi wonyenga kupambana zinthu zonse

10“Ine Yehova ndimafufuza mtima

11Munthu amene amapeza chuma mwachinyengo

12Nyumba yathu yopemphereramo ili ngati mpando waufumu waulemerero

13Inu Yehova, chiyembekezo cha Israeli,

14Inu Yehova, chiritseni, ndipo ndidzachira;

15Anthu akumandinena kuti,

16Ine sindinakuwumirizeni kuti muwalange.

17Musandichititse mantha;

18Ondizunza anga achite manyazi,

19Yehova anandiwuza kuti, “Pita ukayime pa chipata chodzerapo anthu, chimene mafumu a ku Yuda amalowerapo ndi kutulukirapo. Ukayimenso pa zipata zina zonse za Yerusalemu.

20Ukawawuze kuti, ‘Imvani mawu a Yehova, inu mafumu onse a ku Yuda ndi anthu onse a ku Yuda ndi inu nonse okhala mu Yerusalemu amene mumatulukira pa zipata izi.’

21Yehova akuti: samalani kuti pa tsiku la Sabata musanyamule katundu kapena kulowa naye pa zipata za Yerusalemu.

22Musalowetse katundu mʼnyumba zanu kapena kugwira ntchito pa tsiku la Sabata, koma mulipatule tsiku la Sabatalo, monga ndinalamulira makolo anu.

23Komatu iwo sanandimvere kapena kulabadira. Ndi mitima yawo yowumayo sanamvere kapena kulandira malangizo anga.

24Yehova akuti, ‘Muzimvera Ine ndi kuleka kulowetsa kapena kutulutsa katundu pa zipata za mzinda pa tsiku la Sabata. Muzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika posachita ntchito iliyonse pa tsikuli.

25Mukatero ndiye mafumu anu amene akukhala pa mpando wa Davide adzatulukira pa zipata za mzindawu pamodzi ndi nduna zawo. Iwo pamodzi ndi nduna zawo azidzalowa atakwera magaleta ndi akavalo, akuperekezedwa ndi anthu a ku Yuda ndi amene amakhala mu Yerusalemu, ndipo mu mzinda muno mudzakhala anthu mpaka muyaya.

26Anthu adzabwera kuchokera ku mizinda ya Yuda ndi ku midzi yozungulira Yerusalemu, kuchokera ku dziko la Benjamini ndi ku mapiri a kumadzulo, kuchokera ku dziko la mapiri ndi ku Negevi. Adzabwera ndi nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi za chakudya, nsembe za lubani ndi zopereka zachiyamiko ku nyumba ya Yehova.

27Koma ngati simundimvera; mukapanda kusunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika ndi kumanyamula katundu nʼkumalowa naye pa zipata za Yerusalemu pa tsikuli, Ine ndidzabutsa moto pa zipata za Yerusalemu. Moto umenewo udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu ndipo moto wake sudzazima.’ ”

← Yeremiya 16 Yeremiya Yeremiya 18 →