1“Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba
2Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake,
3Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo?
4Kodi idzachita nawe mgwirizano
5Kodi udzasewera nayo ngati mbalame,
6Kodi anthu adzayitsatsa malonda?
7Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga,
8Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo,
9Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza;
10Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa.
11Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere?
12“Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho,
13Ndani angasende chikopa chake?
14Ndani angatsekule kukamwa kwake,
15Kumsana kwake kuli mizere ya mamba
16Mambawo ndi olukanalukana
17Ndi olumikizanalumikizana;
18Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali;
19Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo
20Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi
21Mpweya wake umayatsa makala,
22Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake;
23Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo
24Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala,
25Ngʼonayo ikangovuwuka,
26Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu,
27Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe
28Muvi sungathe kuyithawitsa,
29Zibonga zimakhala ngati ziputu;
30Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo
31Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali,
32Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee,
33Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho,
34Chimanyoza nyama zina zonse;