1Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa.
2Ndipo Yobu anati:
3“Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe
4Tsiku limenelo lisanduke mdima;
5Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli;
6Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani;
7Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino;
8Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo,
9Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima;
10Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga
11“Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa
12Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo
13Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere;
14pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi,
15pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide,
16Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale,
17Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto,
18A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere;
19Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko,
20“Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto,
21kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera,
22amene amakondwa ndi kusangalala
23Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu
24Mʼmalo moti ndidye, ndimalira,
25Chimene ndinkachiopa chandigwera;
26Ndilibe mtendere kapena bata,