1Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
2“Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe
3Ndikumva kudzudzula kondinyoza,
4“Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale,
5kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha,
6Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba
7iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe;
8Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso,
9Diso limene linamuona silidzamuonanso;
10Ana ake adzabwezera zonse
11Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake
12“Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake
13ngakhale salola kuzilavula,
14koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake;
15Adzachisanza chuma chimene anachimeza;
16Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo
17Sadzasangalala ndi timitsinje,
18Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya;
19Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo;
20“Chifukwa choti umbombo wake sutha,
21Palibe chatsala kuti iye adye;
22Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera;
23Akadya nʼkukhuta,
24Ngakhale athawe mkondo wachitsulo,
25Muviwo adzawutulutsira ku msana,
26mdima wandiweyani ukudikira chuma chake.
27Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake;
28Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake,
29Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa,