1Kodi ndani uyo akubwera kuchokera ku Edomu,
2Nanga bwanji zovala zanu zili psuu,
3“Ndapondereza ndekha anthu a mitundu ina ngati mphesa,
4Pakuti ndinatsimikiza mu mtima mwanga kuti lafika tsiku lolipsira anthu anga;
5Ndinayangʼana ndipo panalibe munthu wondithandiza.
6Ndinapondereza mitundu ya anthu ndili wokwiya;
7Ndidzafotokoza za kukoma mtima kwa Yehova,
8Yehova anati, “Ndithu awa ndi anthu anga,
9Iyenso anasautsidwa mʼmasautso awo onse,
10Komabe iwo anawukira
11Pamenepo anthu ake anakumbukira masiku amakedzana,
12Ali kuti amene anachita zinthu zodabwitsa
13amene anawayendetsa pa nyanja yozama?
14Mzimu Woyera unawapumulitsa
15Inu Yehova amene muli kumwambako, pa mpando wanu wolemekezeka,
16Koma Inu ndinu Atate athu,
17Chifukwa chiyani, Inu Yehova, mukutisocheretsa pa njira zanu?
18Anthu anu atangokhala pa malo anu opatulika pa kanthawi kochepa,
19Ife tili ngati anthu amene