1Yehova anandiyankhula nati:
2“Iwe mwana wa munthu, iwuze mfumu ya ku Turo mawu a Ine Ambuye Yehova akuti,
3Taona, ndiwedi wanzeru kupambana Danieli.
4Mwa nzeru zako ndi kumvetsa kwako
5Ndi nzeru zako zochitira malonda
6“ ‘Choncho Ine Ambuye Yehova ndikuti,
7Ine ndidzabwera ndi anthu achilendo, anthu ankhanza,
8Iwo adzakuponyera ku dzenje
9Kodi udzanenabe kuti, ‘Ine ndine mulungu,’
10Udzafa imfa ya anthu osachita mdulidwe
11Yehova anandiyankhula kuti:
12“Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira mfumu ya Turo ndipo uyiwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti,
13Iwe unkakhala ngati mu Edeni,
14Ndinayika kerubi kuti azikulondera.
15Makhalidwe ako anali abwino
16Unatanganidwa ndi zamalonda.
17Unkadzikuza mu mtima mwako
18Ndi malonda ako achinyengo unachulukitsa machimo ako.
19Anthu onse amitundu amene ankakudziwa
20Yehova anandiyankhula nati:
21“Iwe mwana wa munthu, utembenukire ku mzinda wa Sidoni ndipo unenere mowudzudzula kuti,
22‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,
23Ndidzatumiza mliri pa iwe
24“ ‘Nthawi imeneyo Aisraeli sadzakhalanso ndi anthu pafupi achipongwe amene ali ngati nthula zowawa ndi ngati minga zopweteka. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.
25“ ‘Ine Ambuye Yehova mawu anga ndi awa: Nditasonkhanitsa Aisraeli kuchoka ku mayiko kumene anamwazikira, ndidzadzionetsa kuti ndine woyera pakati pawo pamaso pa anthu a mitundu ina. Adzakhala mʼdziko lawo, limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo.
26Adzakhala kumeneko mwamtendere ndipo adzamanga nyumba ndi kulima minda ya mpesa. Adzakhala kumeneko mwamtendere pamene ndidzalange anthu oyandikana nawo, amene ankawanyoza. Motero iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.’ ”