We Believe JesusFé, Esperança e Nova Vida

Ahebri 1

Biblica® Tsekulani Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero · nianja

Ahebri Ahebri 2 →

1Kale lija Mulungu ankayankhula ndi makolo athu pa nthawi zosiyanasiyana ndiponso mwa njira zosiyanasiyana kudzera mwa aneneri.

2Koma masiku otsiriza ano, Mulungu wayankhula nafe kudzera mwa Mwana wake. Mwanayu anamusankha kuti akhale mwini wa zinthu zonse, ndiponso Mulungu analenga dziko lonse kudzera mwa Iye.

3Mwanayo ndiye kuwala kwa ulemerero wa Mulungu, chithunzithunzi chenicheni cha khalidwe lake. Iyeyu amachirikiza zinthu zonse ndi mphamvu ya mawu ake. Iye atayeretsa anthu kuchoka ku machimo awo, anakhala pansi kumwamba kudzanja lamanja la Mulungu waulemerero.

4Mwanayu ndi wamkulu koposa angelo, monga momwe dzina limene analandira limaposa dzina la angelo.

5Kodi ndi kwa mngelo uti, kumene Mulungu anati,

6Pamene Mulungu amatuma Mwana wake woyamba kubadwa ku dziko lapansi anati,

7Iye ponena za angelo akuti,

8Koma za Mwana wake akuti,

9Mwakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa;

10Mulungu akutinso,

11Zimenezi zidzatha, koma Inu ndinu wachikhalire.

12Mudzazipindapinda ngati chofunda;

13Kodi ndi kwa Mngelo uti kumene Mulungu ananenapo kuti,

14Kodi angelo onse si mizimu yotumikira odzalandira chipulumutso?

Ahebri Ahebri 2 →