1Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti?
3Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama?
4Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu,
5Koma utayangʼana kwa Mulungu,
6ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima
7Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa
8“Funsa kwa anthu amvulazakale
9pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse,
10Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera?
11Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho?
12Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula;
13Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu;
14Kulimba mtima kwake kumafowoka;
15Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka;
16Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa,
17mizu yake imayanga pa mulu wa miyala
18Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo,
19Ndithudi chomeracho chimafota,
20“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa
21Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete
22Adani ako adzachita manyazi,