1“Ndinachita pangano ndi maso anga
2Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani?
3Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa,
4Kodi Mulungu saona zochita zanga,
5“Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso,
6Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama
7ngati mayendedwe anga asempha njira,
8Pamenepo ena adye zimene ndinadzala,
9“Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi,
10pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya,
11Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi,
12Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko;
13“Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi,
14ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa?
15Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo?
16“Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba,
17ngati chakudya changa ndinadya ndekha,
18chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake,
19ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa,
20ndipo ngati iyeyo sananditamandepo
21ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye,
22pamenepo phewa langa lipokonyeke,
23Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu,
24“Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma
25ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri,
26ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala,
27ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo
28pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo,
29“Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga,
30ine sindinachimwe ndi pakamwa panga
31ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti,
32Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse,
33ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena,
34chifukwa choopa gulu la anthu,
35“Aa, pakanakhala wina wondimva!
36Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa,
37Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita;
38“Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine
39ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama
40pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu