1Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
2“Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi,
3pamene nyale yake inkandiwunikira
4Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri,
5nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane,
6pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka,
7“Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda
8anyamata amati akandiona ankapatuka
9atsogoleri ankakhala chete
10anthu otchuka ankangoti duu,
11Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga,
12chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo,
13Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa;
14Chilungamo chinali ngati chovala changa;
15Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya;
16Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi;
17Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa
18“Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga,
19Mizu yanga idzatambalalira ku madzi,
20Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine,
21“Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi,
22Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso;
23Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula
24Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira;
25Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu;