1Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
2“Imvani mawu anga, inu anthu anzeru;
3Pakuti khutu limayesa mawu
4Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera;
5“Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa,
6Ngakhale ndine wolungama mtima,
7Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani,
8Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa;
9Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu
10“Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu.
11Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake;
12Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa,
13Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani?
14Mulungu akanakhala ndi maganizo
15zamoyo zonse zikanawonongekeratu
16“Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi;
17Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira?
18Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’
19Iye sakondera akalonga
20Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku;
21“Maso a Mulungu amapenya njira za munthu;
22Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani
23Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu,
24Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu
25Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo
26Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo,
27Chifukwa anasiya kumutsata
28Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake,
29Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa?
30kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza,
31“Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti,
32ndiphunzitseni zimene sindikuziona
33Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira,
34“Anthu omvetsa zinthu adzakambirana,
35‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru;
36Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto
37Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira;