1Ndipo Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
2“Ndithu pali Mulungu wamoyo, amene wakana kundiweruza molungama,
3nthawi zonse pamene ndili ndi moyo,
4pakamwa panga sipadzatuluka mawu oyipa,
5Sindidzavomereza kuti inu mukunena zoona;
6Ndidzasunga chilungamo changa ndipo sindidzalola kuti chindichokere;
7“Mdani wanga akhale ngati woyipa,
8Nanga chiyembekezo cha munthu wosapembedza nʼchiyani pamene aphedwa,
9Kodi Mulungu amamva kulira kwake
10Kodi adzapeza chikondwerero mwa Wamphamvuzonse?
11“Ndidzakuphunzitsani za mphamvu ya Mulungu ndipo
12Inu mwadzionera nokha zonsezi.
13“Pano pali chilango chimene Mulungu amasungira woyipa,
14Angakhale ana ake achuluke chotani adzaphedwa ndi lupanga ndipo
15Amene adzatsalireko adzafa ndi mliri,
16Ngakhale aunjike siliva ngati fumbi,
17zimene wasungazo wolungama ndiye adzavale,
18Nyumba imene akuyimanga ili ngati mokhala kadziwotche,
19Amapita kokagona ali wolemera koma kutha kwake nʼkomweko;
20Zoopsa zimamukokolola ngati madzi achigumula;
21Mphepo ya kummawa imamuwulutsa ndipo iye saonekanso ndipo
22Imakuntha pa iye osamuchitira chisoni,
23Mphepoyo imamuwomba ndithu