1Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2“Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi?
3Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe
4Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako,
5“Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa;
6Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima;
7Mayendedwe ake amgugu azilala;
8Mapazi ake amulowetsa mu ukonde
9Msampha wamkola mwendo;
10Amutchera msampha pansi mobisika;
11Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse,
12Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala,
13Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse;
14Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira,
15Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo;
16Mizu yake ikuwuma pansi
17Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi;
18Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima,
19Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake,
20Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake;
21Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa;