We Believe JesusFé, Esperança e Nova Vida

Nehemiya 7

Biblica® Tsekulani Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero · nianja

← Nehemiya 6 Nehemiya Nehemiya 8 →

1Khoma linamangidwa ndipo zitseko zinayikidwa. Pambuyo pake alonda a Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo ndiponso Alevi anasankhidwa.

2Kenaka ine ndinasankha mʼbale wanga Hanani pamodzi ndi Hananiya woyangʼanira nsanja yankhondo kukhala olamulira Yerusalemu chifukwa iyeyu anali munthu odalirika ndi woopa Mulungu kuposa anthu ena.

3Ine ndinawawuza kuti, “Musalole kuti zipata za Yerusalemu zitsekulidwe mpaka dzuwa litatentha, ndipo alonda asanaweruke aonetsetse kuti atseka zitseko ndi kuzipiringidza. Musankhe alonda pakati pa anthu okhala mu Yerusalemu, ena akhale pa malo pawo ndi ena akhale moyangʼanana ndi nyumba zawo.”

4Tsono mzinda wa Yerusalemu unali wotambasuka ndiponso waukulu koma munali anthu ochepa ndipo nyumba zinali zisanamangidwe.

5Ndipo Mulungu wanga anayika mu mtima mwanga maganizo oti ndisonkhanitse anthu olemekezeka, akuluakulu ndi anthu onse kuti alembetse mayina mwa mabanja awo. Ndinapeza buku limene munalembedwa mayina a mabanja a iwo amene anayamba kubwera kuchokera ku ukapolo. Izi ndi zimene ndinazipeza zitalembedwa mʼmenemo:

6Awa ndi anthu a mʼchigawo cha Yuda amene anabwerera kuchokera ku ukapolo amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawatenga ukapolo. Iwo anabwerera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, aliyense ku mzinda wa makolo ake.

7Anabwera pamodzi ndi atsogoleri awa: Zerubabeli, Yesuwa, Nehemiya, Azariya, Raamiya, Nahamani, Mordekai, Bilisani, Misipereti, Bigivai, Nehumu ndi Baana.

8Zidzukulu za Parosi

9Zidzukulu za Sefatiya

10Zidzukulu za Ara

11Zidzukulu za Pahati-Mowabu (kudzera mu mʼbado wa Yesuwa ndi Yowabu)

12Zidzukulu za Elamu

13Zidzukulu za Zatu

14Zidzukulu za Zakai

15Zidzukulu za Binuyi

16Zidzukulu za Bebai

17Zidzukulu za Azigadi

18Zidzukulu za Adonikamu

19Zidzukulu za Abigivai

20Zidzukulu za Adini

21Zidzukulu za Ateri (kudzera mwa Hezekiya)

22Zidzukulu za Hasumu

23Zidzukulu za Bezayi

24Zidzukulu za Harifu

25Zidzukulu za Gibiyoni

26Anthu a ku Betelehemu ndi Netofa

27Anthu a ku Anatoti

28Anthu a ku Beti-Azimaveti

29Anthu a ku Kiriati Yeyarimu Kefira ndi Beeroti

30Anthu a ku Rama ndi Geba

31Anthu a ku Mikimasi

32Anthu a ku Beteli ndi Ai

33Anthu a ku Nebo winayo

34Ana a Elamu wina

35Zidzukulu za Harimu

36Zidzukulu za Yeriko

37Zidzukulu za Lodi, Hadidi ndi Ono

38Zidzukulu za Senaya

39Ansembe anali awa:

40Zidzukulu za Imeri

41Zidzukulu za Pasi-Huri

42Zidzukulu za Harimu

43Alevi anali awa:

44Anthu oyimba:

45Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa:

46Anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu anali awa:

47Zidzukulu Kerosi, zidzukulu za Siya, zidzukulu za Padoni

48Zidzukulu za Lebana za Hagaba, ndi za Salimayi,

49Zidzukulu za Hanani, zidzukulu za Gideli, zidzukulu za Gahari,

50Zidzukulu za Reyaya, zidzukulu za Rezini, zidzukulu za Nehoda,

51Zidzukulu za Gazamu, zidzukulu za Uza, zidzukulu za Paseya,

52Zidzukulu za Besai, zidzukulu za Meunimu, zidzukulu za Nefusimu,

53Zidzukulu za Bakibuku, zidzukulu za Hakufa, zidzukulu za Harihuri,

54Zidzukulu za Baziliti, zidzukulu za Mehida, zidzukulu za Harisa,

55Zidzukulu za Barikosi, zidzukulu za Sisera, zidzukulu za Tema

56Zidzukulu za Neziya, ndi zidzukulu za Hatifa.

57Zidzukulu za antchito a Solomoni:

58zidzukulu za Yaala, zidzukulu za Darikoni, zidzukulu za Gideli,

59zidzukulu za Sefatiya, zidzukulu za Hatilu

60Anthu onse ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi zidzukulu za antchito a Solomoni analipo

61Ali munsiwa anachokera ku Teli-Mela, Teri-Harisa, Kerubi, Adoni, ndi Imeri, koma sanathe kunena mwa tchutchutchu kuti makolo awo kapena mafuko awo analidi Aisraeli kapena ayi.

62Zidzukulu za

63Ndiponso ena pakati pa ansembe anali awa:

64Iwowa anafufuzafufuza mayina awo mʼbuku la mibado ya mabanja awo ndipo sanapeze mayina awo kotero anachotsedwa pa unsembe nawerengedwa ngati odetsedwa pa chipembedzo.

65Choncho bwanamkubwa anawawuza anthuwo kuti asamadye nawo chakudya china chilichonse choperekedwa kwa Mulungu mpaka patapezeka wansembe wodziwa kugwiritsa bwino ntchito ya Urimu ndi Tumimu.

66Chiwerengero chonse cha anthuwa chinali 42,360.

67Kuwonjezera pamenepa panali antchito awo aamuna ndi aakazi 7,337 ndiponso anthu aamuna ndi aakazi oyimba nyimbo okwanira 245.

68Panali akavalo 736, abulu angʼonoangʼono 245.

69Ngamira zawo zinalipo 435 ndipo abulu analipo 6,720.

70Atsogoleri ena a mabanja anapereka mphatso zothandizira ntchito. Bwanamkubwa anapereka ku thumba losungira chuma, ndalama zagolide za makilogalamu asanu ndi atatu, mabeseni makumi asanu ndi zovala za ansembe 530.

71Atsogoleri ena amabanja anapereka ku thumba losungira chuma ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndiponso ndalama za siliva zokwana makilogalamu 1,250.

72Anthu ena onse otsala anapereka ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndalama za siliva zokwana makilogalamu 140, ndiponso zovala za ansembe 67.

73Choncho ansembe, Alevi, alonda a Nyumba ya Mulungu, anthu oyimba nyimbo, ena mwa anthu wamba, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi Aisraeli ena onse ankakhala mʼmizinda yawo.

← Nehemiya 6 Nehemiya Nehemiya 8 →