1Khoma linamangidwa ndipo zitseko zinayikidwa. Pambuyo pake alonda a Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo ndiponso Alevi anasankhidwa.
2Kenaka ine ndinasankha mʼbale wanga Hanani pamodzi ndi Hananiya woyangʼanira nsanja yankhondo kukhala olamulira Yerusalemu chifukwa iyeyu anali munthu odalirika ndi woopa Mulungu kuposa anthu ena.
3Ine ndinawawuza kuti, “Musalole kuti zipata za Yerusalemu zitsekulidwe mpaka dzuwa litatentha, ndipo alonda asanaweruke aonetsetse kuti atseka zitseko ndi kuzipiringidza. Musankhe alonda pakati pa anthu okhala mu Yerusalemu, ena akhale pa malo pawo ndi ena akhale moyangʼanana ndi nyumba zawo.”
4Tsono mzinda wa Yerusalemu unali wotambasuka ndiponso waukulu koma munali anthu ochepa ndipo nyumba zinali zisanamangidwe.
5Ndipo Mulungu wanga anayika mu mtima mwanga maganizo oti ndisonkhanitse anthu olemekezeka, akuluakulu ndi anthu onse kuti alembetse mayina mwa mabanja awo. Ndinapeza buku limene munalembedwa mayina a mabanja a iwo amene anayamba kubwera kuchokera ku ukapolo. Izi ndi zimene ndinazipeza zitalembedwa mʼmenemo:
6Awa ndi anthu a mʼchigawo cha Yuda amene anabwerera kuchokera ku ukapolo amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawatenga ukapolo. Iwo anabwerera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, aliyense ku mzinda wa makolo ake.
7Anabwera pamodzi ndi atsogoleri awa: Zerubabeli, Yesuwa, Nehemiya, Azariya, Raamiya, Nahamani, Mordekai, Bilisani, Misipereti, Bigivai, Nehumu ndi Baana.
8Zidzukulu za Parosi
9Zidzukulu za Sefatiya
10Zidzukulu za Ara
11Zidzukulu za Pahati-Mowabu (kudzera mu mʼbado wa Yesuwa ndi Yowabu)
12Zidzukulu za Elamu
13Zidzukulu za Zatu
14Zidzukulu za Zakai
15Zidzukulu za Binuyi
16Zidzukulu za Bebai
17Zidzukulu za Azigadi
18Zidzukulu za Adonikamu
19Zidzukulu za Abigivai
20Zidzukulu za Adini
21Zidzukulu za Ateri (kudzera mwa Hezekiya)
22Zidzukulu za Hasumu
23Zidzukulu za Bezayi
24Zidzukulu za Harifu
25Zidzukulu za Gibiyoni
26Anthu a ku Betelehemu ndi Netofa
27Anthu a ku Anatoti
28Anthu a ku Beti-Azimaveti
29Anthu a ku Kiriati Yeyarimu Kefira ndi Beeroti
30Anthu a ku Rama ndi Geba
31Anthu a ku Mikimasi
32Anthu a ku Beteli ndi Ai
33Anthu a ku Nebo winayo
34Ana a Elamu wina
35Zidzukulu za Harimu
36Zidzukulu za Yeriko
37Zidzukulu za Lodi, Hadidi ndi Ono
38Zidzukulu za Senaya
39Ansembe anali awa:
40Zidzukulu za Imeri
41Zidzukulu za Pasi-Huri
42Zidzukulu za Harimu
43Alevi anali awa:
44Anthu oyimba:
45Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa:
46Anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu anali awa:
47Zidzukulu Kerosi, zidzukulu za Siya, zidzukulu za Padoni
48Zidzukulu za Lebana za Hagaba, ndi za Salimayi,
49Zidzukulu za Hanani, zidzukulu za Gideli, zidzukulu za Gahari,
50Zidzukulu za Reyaya, zidzukulu za Rezini, zidzukulu za Nehoda,
51Zidzukulu za Gazamu, zidzukulu za Uza, zidzukulu za Paseya,
52Zidzukulu za Besai, zidzukulu za Meunimu, zidzukulu za Nefusimu,
53Zidzukulu za Bakibuku, zidzukulu za Hakufa, zidzukulu za Harihuri,
54Zidzukulu za Baziliti, zidzukulu za Mehida, zidzukulu za Harisa,
55Zidzukulu za Barikosi, zidzukulu za Sisera, zidzukulu za Tema
56Zidzukulu za Neziya, ndi zidzukulu za Hatifa.
57Zidzukulu za antchito a Solomoni:
58zidzukulu za Yaala, zidzukulu za Darikoni, zidzukulu za Gideli,
59zidzukulu za Sefatiya, zidzukulu za Hatilu
60Anthu onse ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi zidzukulu za antchito a Solomoni analipo
61Ali munsiwa anachokera ku Teli-Mela, Teri-Harisa, Kerubi, Adoni, ndi Imeri, koma sanathe kunena mwa tchutchutchu kuti makolo awo kapena mafuko awo analidi Aisraeli kapena ayi.
62Zidzukulu za
63Ndiponso ena pakati pa ansembe anali awa:
64Iwowa anafufuzafufuza mayina awo mʼbuku la mibado ya mabanja awo ndipo sanapeze mayina awo kotero anachotsedwa pa unsembe nawerengedwa ngati odetsedwa pa chipembedzo.
65Choncho bwanamkubwa anawawuza anthuwo kuti asamadye nawo chakudya china chilichonse choperekedwa kwa Mulungu mpaka patapezeka wansembe wodziwa kugwiritsa bwino ntchito ya Urimu ndi Tumimu.
66Chiwerengero chonse cha anthuwa chinali 42,360.
67Kuwonjezera pamenepa panali antchito awo aamuna ndi aakazi 7,337 ndiponso anthu aamuna ndi aakazi oyimba nyimbo okwanira 245.
68Panali akavalo 736, abulu angʼonoangʼono 245.
69Ngamira zawo zinalipo 435 ndipo abulu analipo 6,720.
70Atsogoleri ena a mabanja anapereka mphatso zothandizira ntchito. Bwanamkubwa anapereka ku thumba losungira chuma, ndalama zagolide za makilogalamu asanu ndi atatu, mabeseni makumi asanu ndi zovala za ansembe 530.
71Atsogoleri ena amabanja anapereka ku thumba losungira chuma ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndiponso ndalama za siliva zokwana makilogalamu 1,250.
72Anthu ena onse otsala anapereka ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndalama za siliva zokwana makilogalamu 140, ndiponso zovala za ansembe 67.
73Choncho ansembe, Alevi, alonda a Nyumba ya Mulungu, anthu oyimba nyimbo, ena mwa anthu wamba, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi Aisraeli ena onse ankakhala mʼmizinda yawo.