1Nayi mbiri ya ana a Nowa, Semu, Hamu ndi Yafeti. Ana atatuwa anabereka ana awo chitatha chigumula.
2Ana aamuna a Yafeti anali:
3Ana aamuna a Gomeri anali:
4Ana aamuna a Yavani anali:
5(Amenewa ndiwo makolo a anthu okhala mʼmphepete mwa nyanja. Awa ndi ana a Yafeti monga mwa mafuko a mu mitundu yawo, uliwonse ndi chiyankhulo chake).
6Ana aamuna a Hamu anali:
7Ana aamuna a Kusi anali:
8Kusi anabereka Nimurodi amene anali wankhondo wamphamvu kwambiri pa dziko lapansi.
9Iye anali mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova; nʼchifukwa chake anthu ali ndi chisudzo, chakuti, “Ndiwe mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova monga Nimurodi.”
10Malo oyambirira a ufumu wake anali Babeli, Ereki, Akadi ndi Kaline. Malo onsewa anali mʼdziko la Sinara.
11Atachoka mʼdziko limeneli anapita ku Asiriya kumene anakamanga Ninive, Rehoboti-Iri, Kala,
12ndi Reseni, mzinda waukulu umene uli pakati pa Ninive ndi Kala.
13Igupto ndiye kholo la
14Apaturusi, Akasilu ndi Akafitori (kumene kunachokera Afilisti).
15Kanaani anabereka mwana wake wachisamba,
16Ayebusi, Aamori, Agirigasi;
17Ahivi, Aariki, Asini,
18Aaravadi, Azemari ndi Ahamati.
19mpaka ku malire a Kanaani. Malirewo anachokera ku Sidoni kulowa cha ku Gerari mpaka ku Gaza, ndi kulowa ku Sodomu, Gomora, Adima ndi Zeboimu mpaka ku Lasa.
20Amenewa ndiwo ana aamuna a Hamu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe amakhala ndi mitundu yawo.
21Semu amene anali mkulu wake wa Yafeti nayenso anabereka nakhala kholo la Eberi.
22Ana aamuna a Semu anali:
23Ana aamuna a Aramu anali:
24Aripakisadi anabereka Sela,
25A Eberi anabereka ana aamuna awiri:
26Yokitani anabereka
27Hadoramu, Uzali, Dikila,
28Obali, Abimaeli, Seba,
29Ofiri, Havila ndi Yobabu. Onsewa anali ana aamuna a Yokitani.
30Chigawo chimene ankakhala chinayambira ku Mesa mpaka ku Seferi, ku dera la mapiri chakummawa.
31Amenewa ndiwo ana a Semu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe ankakhala ndi mitundu yawo.
32Amenewa ndiwo mafuko a ana aamuna a Nowa monga mwa mibado ya mitundu yawo. Mitundu yonse ya anthu inatuluka mwa iwowa ndi kufalikira pa dziko lonse lapansi chitatha chigumula chija.