1Mawu a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya ku Yerusalemu:
2“Zopandapake! Zopandapake!”
3Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zake zonse
4Mibado imabwera ndipo mibado imapita,
5Dzuwa limatuluka ndipo dzuwa limalowa
6Mphepo imawombera cha kummwera
7Mitsinje yonse imakathira ku nyanja,
8Zinthu zonse ndi zotopetsa,
9Zomwe zinalipo kale zidzakhalaponso,
10Kodi chilipo chinthu chimene wina anganene kuti,
11Anthu akale sakumbukiridwa,
12Ine, Mlalikine, ndinali mfumu ya Israeli mu Yerusalemu.
13Ndinayika mtima wanga pophunzira ndi kufunafuna mwa nzeru zinthu zonse zimene zimachitika pansi pa thambo. Ndi ntchito yolemetsa ndithu imene Mulungu anayipereka kwa anthu!
14Ine ndaona zinthu zonse zochitika pansi pano; zinthu zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
15Chinthu chokhota sichingathe kuwongoledwa;
16Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Taona, ine ndakula ndi kukhala wa nzeru zochuluka kupambana aliyense amene analamulirapo Yerusalemu ndisanabadwe; ndaphunzira nzeru zochuluka ndi luntha.”
17Ndipo ndinadzipereka kuti ndithe kumvetsa kuti nzeru nʼchiyani, misala nʼchiyani, uchitsiru nʼchiyani, koma ndinazindikira ichi, kuti kuteronso nʼkungodzivuta chabe.
18Pakuti nzeru zochuluka zimabweretsa chisoni chochulukanso: